Latest quotes | Random quotes | Vote! | Latest comments | Submit quote

Talent wednesday

MPHATSO ZA MZIMU WOYERA

Wolemba: Innocent Masina Nkhonyo 30th July,2008

SENDERANI chifupi makosana ndi madona inu
Ndikupakulireni wa mzimu woyera mtakura
Ndiye atilengera maphata a wotenderedwa bwino maluso
kasupe wa za awoo zachikhakhali ntchedzero
mmisiri wa tsimba la wothyakuka bwino malangizo
Ngati wopota kabula
Wobwitimizidwa ndi Deneka wa khekhekhe
Ndiye atimangira mauvuni wowotchera zikondamoyo za matamando
Atilukira mathungwa mzimu woyera
Wotchezera chidulocha athu mayamiko kwa Mphambe Mulungu wa Mbona
Kudzera mu wombwandira chidwiwo athu maluso

Muyitaneni Phwendule
Thobwa la ulaliki adzatsope nawo mbamba
Ndinena wothethetsedwa mokankha mwazi uthenga
Ndi awo woyera kuda nakufuna a Juliano Kanyongolo
Poti nawo mchikhatho anawafumbatitsa yozunazunatu mphatso
Si inanso koma ija yofwanthamula loyera lemba

wisuwisu nkhope inali ndwii Nasuwandeyu
waphethira atasusa lake philikaniro
Mu msuzi wa mingoli ya magitala
Ndinena msambo zokwidzingwidwa ndi wathuyo mngelezi Paul Naluso
ummhu wa luso ati nanga wake mfunda

Athawatu kwa a Nebaku anawa
Zitawapeza zonyamula moyo ng’oma
Za ija yotsitsimutsa kwaya ndinena ya Chanco Catholic mboba inu
Poti nawonso ali nalo luso
Mbamba ya mzimu woyera mphatso anambwandira nawo
Jealous down nkhululu sasiya msuzi mtakuwuzani
Tilinayo ya maluso mitunga
Adatiwedzera mzimu woyera
Awo zachita tewa zifuwa ndi ija ya ndimanga khwekhwe nkhawa
Alikitimulireni uja wothambitsa msunamo gule
Poti yanu ija yotakasa chiuno mphatso
Adakuninkhanitu Yahweh, kuti osasanthidwa ndi nkhawa azanu
inu muwathuzitse chawo chimkankha mwazi

Awatu asiya zili gadaa m’mbale nthumbwana
Anyezi akuchita fulukutufulukutu mumsuzi wonyenzimira ngati kalilore
Nawo ati kudzafwanthamula sitepe
Litawambwandira chidwi la Yamikani liwu uko ku YCS
paja nayenso ali nalo lake luso
lofulula chitukwi cha mayimbidwe


Akakhala a Piringu ndimiteshi athobotsa uja tameki amati abwire
Atakumanizana nazo gululu
zobalalitsa nkhawa nthabwala
ndinenatu za Stella wokulumunya mawu inu,
mbamba mopatsadi kaso mwa chake chija chiwongo

Msonkhemsonkhe tichite tsono madona ndi Madoda inu
Athu mapemphero madengu titadendekera kwa a Tate
Kuti ena akholophethe maluso, Mbamba atininkhe
ija yathu nkhoswe
Ndinenatu mzimu woyera, inu atitumizire
Inunsotu muli nawo maluso baba
Mutiwonetse umo muvinira miyendo ili paphewa
Poti nkwanuko kuwonetsa luso
Mudzathira nsembe ya chiyamiko kwa uyo Tate
Wotigawira futali wa MALUSO
Tsono wonetsani lero mayi, lanu lija luso


To the greater glory of God, the Father, Tthe Son
and The Holy Spirit from whom all our talents come.

poem by Report problemRelated quotes
Added by Poetry Lover
Comment! | Vote! | Copy!

Share
 
 

No comments until now.


Comment

Name (required)

E-mail address (hidden)

Search


Recent searches | Top searches